Masalimo 150

Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu. Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana. Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze. Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro. Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri. Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.

Buku Lopatulika (Chichewa)

copyright © 2016, 2002 Biblica, Inc — CC-BY-SA-4.0 — CC-BY-SA-4.0

뉴스레터 구독

새로운 프로필과 행사, 플랫폼 소식을 받아 보세요.