Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.