Masalimo 122

Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.” Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu. Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi. Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova. Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide. Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino. Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.” Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.” Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

Buku Lopatulika (Chichewa)

copyright © 2016, 2002 Biblica, Inc — CC-BY-SA-4.0 — CC-BY-SA-4.0

뉴스레터 구독

새로운 프로필과 행사, 플랫폼 소식을 받아 보세요.