Masalimo 3

Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira! Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” Sela Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula. Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. Sela Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza. Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse. Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. Sela

Buku Lopatulika (Chichewa)

copyright © 2016, 2002 Biblica, Inc — CC-BY-SA-4.0 — CC-BY-SA-4.0

Abonner på nyhetsbrevet vårt

Hold deg oppdatert på nye profiler, arrangementer og plattformnyheter.